Odalitsika

Odalitsika

Share

15/10/2025

Unduna woona za ubale wadziko lino ndi maiko ena watsimikiza kuti a Malawi 22 anali mu bus yomwe inachita ngozi ndikupha anthu oposela 40 Lamulungu usiku mu dera la Limpopo, ku South Africa.

Mu kalata yomwe yatuluka Lachiwiri usiku, undunawu wati wazindikira a Malawi 14 pomwe ena asanu ndi atatu akusowabe. Mwa omwe awazindikilawa, 8 akanali mu chipatala pomwe 6 awatulutsa.

Nyumba yofalitsa mawu ya BBC inalengeza lolemba kuti athu 42 afa pa ngozi ya bus m'mapiri ena pa msewu wa N1 mchigawo cha Limpopo. Bus-yo inali pa ulendo wobwera ku Malawi kudzera ku Zimbabwe, ndipo inanyamula nzika za Malawi ndi Zimbabwe.

Koma unduna-wu mu kalata yake wati anthu 43 ndiwo afa pangoziyo ndipo kuti bus-yo inanyamula anthu oposela 90. Undunawu sunapeze uthenga wa m'Malawi amene wamwalira pangoziyo koma wati akulu akulu a dziko la South Africa akuunikabe matupi kuti awazindikire.

Komabe, m'modzi mwa anthu ogwira ntchito ku ofesi ya kazembe ku South Africa-ko wauza Zodiak Online kuti ndizovuta kuzindikira anthu chifukwa ena analibe ziphaso zowazindikilitsa komanso ziphaso zoyendera.

(by John-Paul Kayuni-Lilongwe: 10/15/25)

15/10/2025

HAPPY MOTHER'S DAY. osaiwala kutipanga follow Odalitsika mulungu amakhalanaye

24/09/2024

BOMA NDILOMWELI PALIBE KUSINTHA

Want your place of worship to be the top-listed Place Of Worship in Lilongwe?
Click here to claim your Sponsored Listing.

Telephone

Website

Address


LILONGWE TO SALIMA
Lilongwe